MALAMULO ENA APA MOWA 1. Lemekezani ogula olo atakhala mwana - TopicsExpress



          

MALAMULO ENA APA MOWA 1. Lemekezani ogula olo atakhala mwana kwainu koma mutcheni mayina monga,afana ofewa, mkuluwanga, achimwene, munthu wankulu, boss, abwana, akumuzi, achibale, reverend ndi ena otelo 2. Peleka moni kwa ogula musanakhale pasi 3. Osayankhula nkhani zambiri kuposa ogula and mvetselani mwachidwi nkhani zaogula olo zili zopanda mutu 4. Onetsesani nthawi zose ogula akaitanisa mowa pa kauntala, pitani mukanyamure ndinu mowawo kapena muuzeni wapano achite changu 5. Ogula akakutumani osanyalanyaza changu pamalo 6. Nyimbo iliyose yomwe ogula waikonda vinani chala mwamba 7. Musaoneke dolo kuposa ogula ngati mwavala bwino akakufusani mungoti ndi kaunjika wa lizulu 8.Osamamwa mowa odula kuposa omwe akumwa ogula 9. Onesesani kuti ogula azimaliza mowa wake wanu usanathe mungazalowe airlock 10. Ngati pagulidwa nyama onesesani kuti ogula akhale oyamba ndi omaliza kutolamo inu limbikilani salad. 11. Ngati ogula akoka onesesani kuti muapezele zishango, Moyo wawo ndiofunika kuti pammawa azaguleso 12. Mutsekulireni mowa ogula nthawi zonse 13. Nthabwala ya ogula ndiyoseketsa kwambiri nthawi zonse chomcho muziseka mpakana misozi -enjoy the weekend always drink responsibly but know God will Punish eti ?
Posted on: Fri, 21 Nov 2014 06:02:59 +0000

Recently Viewed Topics




© 2015