JOSEPHY NKASA WAKWIYA TSOPANO Lyrics :Josefe Mkasa VERSE Chomwe munthu wamkulu akuchiona atakhala pansi Mwana sangachione olo ataimilira Economic recovery plan Malawi yativuta Taonani yayamba kutulutsa minga Mfumu inatiuza kuti potha miyezi 18 Chuma cha dziko la Malawi chiyamba kuyendanso bwino Lero tiku’uzidwa kuti Kwacha yalimba tsopano Iri ndi mphamvu, mukunamiza mafuko Ngati Kwacha iri ndi mphamvu bwanji mitengo ya katundu Ikukwerabe, sikutsika mitengo Mafuta agalimoto akumatsika mtengo Kutsitsa akunenako atsitsa ndi K10 CHORUS KULIRA KWA AMPHAWI KWAMVEKA DZIKO LONSE KULIBE AKUTIMVA AYANG’ANA KUMBALI ONSE PAGULU LAWO AONJEZA MAKANI ATI TIZITAKATA IFE TITAKATA BWANJI? POMWE TIRIBE MPAMBA ZOMWE TIKADALIRA KALE ZIDALEKA KUYENDA VERSE Mayiko anzathu tidayandikana nawo Ndi otukuka, anthu ambiri alemera Mavoti awo adasankha amuna ochita malonda, otha bizinesi Chitsanzo ku Mozambique anthu adavotera ndani? Armando Guebuza munthu wa bizinesi Pa Zambia pomwepa wanthu adavotera ndani? Micheal Sata munthu wa bizinesi Pitani ku mayiko awo mukapeze n’kotukuka Sungayerekeze n’pano pa Nyasaland Nafenso a Malawi tichite chimodzimodzi Tisankhe munthu ochita bizinesi CHORUS KULIRA KWA AMPHAWI KWAMVEKA DZIKO LONSE KULIBE AKUTIMVA AYANG’ANA KUMBALI ONSE PAGULU LAWO AONJEZA MAKANI ATI TIZITAKATA IFE TITAKATA BWANJI? POMWE TIRIBE MPAMBA ZOMWE TIKADALIRA KALE ZIDALEKA KUYENDA Nkasa sadzatheka ayi
Posted on: Wed, 18 Sep 2013 06:53:51 +0000